Mulungu adalitsa Sara/God blesses Sarah

Gawani

Genesis 17:15-27, nthawi yayitali yadutsa Abrahamu wakula mopyola muyezo wobereka mwana ngakhalenso mkazi wake Sara. Mulungu akudalitsa Sara ndipo akuumuza Abrahamu kuti Sara azakhala ndi mwana yemwe azamutcha dzina lake Isake. Mulungu ndi wokhulupirika ndipo akusunga malonjezo ake. Izi zimaonekabe zosamvesetsa kwa Abrahamu chifukwa iye ndi mkazi wake anali atadutsa zaka zoberekera ana. Apa ndi pamene ife Akhristu tikuyenera kumvetsetsa bwino lomwe kunena kuti mulungu amapanga zimene munthu sangakwaniritse nkomwe. Izi ziyenera kutilimbikitsa ife kukhalabe nchoonadi ngakhale mavuto achuluke popeza mulungu wathu amachita zimene munthu sangathe choncho azatilimbikitsa mpaka Yesu azabwere.

Genesis 17:15-27, time has passed and Abraham has passed the age of bearing a child and so is his wife. God blesses Sarah and tells Abraham that Sarah will have a child by this time next year and they will name him Isaac. God is faithful and he keeps his promises. This still seemed impossible to Abraham and Sarah because they had passed the age of bearing a child. Now this is where Christians must learn a very good lesson knowing that God is faithful and he keeps his promises, this assures us all that he will keep us strong until the coming of Jesus the second time. Even when fears are stilled we can be confident and remain in the truth.