Yesu Khristu mwini Chilamulo komanso mpulumutsi wa anthu onse/Jesus Christ the fulfilment of the law and savior of all people

Gawani

Luka 2:21-35 ndime ya malembayi ikukamba zinthu zingapo zomwe ndizofunika kuzikamba. Ndimeyi ikukamba zokhuza Yesu kukhala okwanilitsa chilamulo. Izi zikutheka bwanji? Patapita masiku asanu ndi atatu Yesu atabadwa, makolo ake anapita naye ku Yelusalemu komwe anamuchita mdulidwe monga mwachilamulo cha Mose ndipo anamutcha dzina loti Yesu momwe analonjezera ngelo uja. Izi zinachitika kukwaniritsa malemba. Mavesi omwewa akuwonetsera kuti kubadwa kwa Yesu kunali kukwanilitsidwa kwa malonjezo a mulungu. Ngelo wa mulungu ataonekera kwa Maria anamulonjeza kuti azakhala ndi mwana ndipo mwanayo azamutcha dzina lake Yesu. Mavesi awa akuonetsera kuti zinachitikadi malingana ndi lonjezolo ndipo mwanayo anamutchadi Yesu. Chinthu china chofunikira kudziwa chomwe mavesi awa akukamba ndi ichi, Yesu ndi nkhoswe ya anthu onse okhala pa dziko. Ndime za malembazi zikukamba momveka bwino kuti “mwanayo azakhala kugwa ndi kuzuka  kwa ambiri mu Israeli.” Izi zikuonetsera kuti Yesu ndi nkhoswe ya anthu padziko. Iye ndi njira yokhululukira machimo athu. Nthawi zonse ndime za malemba ngati izi zimatilimbikitsa ife kutsendera chifupi ndi mulungu podzindikira kuti tili ndi nkhoswe yokhululuka machimo athu.
 
Luke 2:21-35 this passage exposes three important things which are worthy discussing. This passage talks about Jesus being the fulfillment of the law. How so? Eight days after Jesus’ birth, his parents took him to Jerusalem where he was circumcised per the law of Moses. And they named him Jesus according to what the angel said they were to name him. This happened in fulfillment of the scriptures. These verses also show that the birth of Jesus happened in fulfillment of promises made by God. After the angel appeared to Mary he promised her that she would give birth to a son and she is to name him Jesus. And these verses show that it happened exactly as the angel promised and Mary and Joseph named the child Jesus. One more thing to take note of from these verses is that Jesus is the propitiatory sacrifice for all people on earth. The verses say that “the child will be the down fall and the rising of the many in Israel.” This clearly paints the picture of the one who atones the sins of the many on earth. He is the way that many sins are forgiven. Every time we learn something like this from the scriptures we are encouraged. It draws us ever closer to God knowing that we have someone who atones for our sins and we can therefore approach the throne of Grace.