Kukhala moyo osogozedwa ndi mzimu woyera/Living by the spirit

Gawani

Genesis 13:1-18 Abramu wapeza chuma chambiri chimene chikumupanga kukhala munthu wolemera kwambiri. Abramu anabwerera kumalo kumene anamanga tenti komanso guwa lansembe ndipo analambira mulungu. Abramu alambilanso Mulungu kuonetsera kudzipereka kwake kwa mulungu. Abramu ndi Loti anapeza chuma chambiri ndipo ogwira ntchito awo anayamba kukangana. Pamenepo Abramu anathetsa nkangano umenewu popereka mwayi kwa Loti kuti asankhe malo amene iye anawakonda, iye anasankha malo omwe anali kunja kwa malonjezo a mulungu. Pamenepa ife ngati akhristu tiyenera kukhala osamalitsa pamene tikupanga chisankho pa nkhani yokhuza malonjezo a mulungu pa anthu ake. Mulungu anatilonjeza moyo wosatha kudzera mwa Yesu Khristu, tiyenera kulorera mzimu woyera kuti atitsogolere momwe anamutsogolera Abramu kukhala okhadzikika mu malonjezo a Mulungu.

Genesis 13:1-18 Abram has accumulated a lot of wealth that is now making him a rich man. Abram returned to the place he first got when he reached the land of Canaan and built an altar for God and he worshipped him there once more and he dedicated himself to God again. Abram and Lot accumulated so much wealth and that brought in arguments between the workers. Abram settled the dispute and gave Lot a chance to choose a place for himself and he chose the land that was outside God’s promises. As christians we need to understand that we have a promise through Jesus Christ. So we need to stay firm and allow the Holy spirit lead us and help us to remain in God’s promises just as he did with Abram.