Mzimu woyera anatsekulira njira anthu amitundu kuti akhulupirire uthenga wabwino/The holy spirit opened the door for gentiles to believe the Gospel

Gawani

Mateyu 5:17-20 Yesu akwera pa Phiri ndipo akhala pansi ndikuyamba kuphunzitsa ophunzira ake ngati Mose watsopano ndi opereka lamulo watsopano. Funso nali, funso limene limazunguza anthu ambiri; kodi ndi ubale wanji omwe ulipo pakati pa lamulo la Khristu ndi la muchipangano chakale? Pofuna kuyankha funso limeneli, chiyambi cha vesi ya 17 ya chaputachi imapereka yankho lomveka bwino. Yesu anti “musaganize kuti ndinabwera kuzathetsa chilamulo ndi aneneri. Sindinabwere kuzathetsa koma kudzakwaniritsa.” Tsopano, chaputa cha 1, 2, 3, 4 cha Mateyu muli zolemba zomwe zimasonyeza kukwaniritsidwa kwa kubwera kwa Mesiya. Mwa chitsanzo, mwana Yesu anatengeredwa ku Igupto pofuna kukwaniritsa zomwe zinalembedwa zonena kuti ‘ndinamuitana mwana wanga kuchoka ku Igupto.’ Izi zikuonetsa kuti Yesu sanabwere kuzathetsa chilamulo ndi aneneri koma kuzakwaniritsa zonse zomwe zinalembedwera iye, zokhuza iye. Koma, kodi chilamulo, aneneri ndi zolembalemba zinangoperekedwa kwa Ayuda popanda chifukwa? Kapena inangokhala njira yonena kuti iwo azizitukumulira? Ayi! Chilamulo komanso aneneri zinaperekedwa kwa iwo ngati njira yowakonzekeretsa za kubwera kwa Mesiya. Ndiye, tinene kuti chilamulo ndi aneneri zikuphunzitsa ife kuti tizinyoza ena omwe samatsatira kadyedwe ka Ayuda? Kapena chifukwa samapembeza tsiku lofanana ndi lomwe inu mumapembezera? Kapena chifukwa samasunga sabata momwe inu mumachitira? Yesu akutitsimikizira kuti anabwera kuzapulumutsa Ayuda ndi Amitundu. Izi zikuoneka bwanji? Mzimu woyera amatsekulira njira amitundu kuti amve ndi kukhulupirira uthenga wabwino wa Yesu Khristu ndikulandira chipulumutso.

 
Matthew 5:17-20 Jesus gets on a mountain and sits down to teach his disciples as the new Moses and the new law giver. Now the question that has many people wonder so much is; what is the relationship of the law of Christ to the law of the old testament? To answer that question, the beginning of verse 17 of this chapter clears our minds with what Jesus himself said. Jesus said “don’t think that I came to abolish the law or the prophets. I did not come to abolish but to fulfill.” Now, chapters 1, 2, 3, 4 of Matthew records all the accounts that took place in fulfilment of the coming of Messiah. For example, baby Jesus was taken to Egypt to fulfill what was written saying that ‘I called my son out of Egypt.’ This shows us that Jesus indeed came to fulfill what was written about him and for him and not to abolish the law and the prophets. But, was the law, the prophets and the writings given to the Jews for no good reason at all? Or was it just for them to brag that they had the law and the prophets? No! the law and the prophets were given them as a way of preparing them for the coming of messiah. So, does the law and the prophets teach us to view others lesser because they’re unable to follow the diet of the Jews? Or because they do not worship on a certain day like you do? Or that they do not keep the Sabbath according to your point of view? Jesus tells us clear that he came to save all, whether Jew or Gentile. Where do we see this? The holy spirit opens the door for Gentiles to hear and believe the Gospel of Jesus Christ and receive salvation.