Mulungu ndi wabwino ndi wolungama/God is good and righteous

Gawani

Genesis 18:16-33 mulungu akuonetsera chilungamo chake pamene anthu akuchita zosutsana naye. Mulungu walinganiza zowononga Sodomu chifukwa cha uchimo wawo koma muzonsezi mulungu akukhalabe olungama. Chifukwa mulungu akuonetsera chilungamo chake mwa Abrahamu, zimene iyeyo ali ngati mulungu kuti iye amadalitsa komanso iye amawononga, iye amatembelera, iye amalanga. Mulungu waonetsera madalitso ake pa Abrahamu pochita naye malonjezo ndi kuwakwaniritsa. Tsopano mulungu akufuna kumuonetsera Abrahamu kuti iye ngati mulungu amalanga onse ochita zoyipa. Kodi ife tikusankha kukondweletsa mulungu kapena zokhumba zathu ndi zomwe zili pa sogolo? Ngati ndi choncho kodi tikudziwa kuti mulungu ndi olungama ndipo sazalora kuti tchimo lipite osalangidwa! Kodi nanga ife tili pati?

Genesis 18:16-33 God shows his great righteousness when people are up against him. God has spoken out the distraction of Sodom because of their great sins and in all of this God remains righteous. God demonstrates his righteousness through Abraham that he blesses, judges and he also curses and he punishes. God has shown his blessings through Abraham by making promises with him and fulfilling them. And now God wants to show Abraham that he punishes those who do sin. Are we choosing to please God or are we putting ourselves in the front? If that’s so, did we know that God is righteous and that he will never let sin go unpunished? Now, where are we found?