Mulungu apulumutsa Loti/God rescues Lot

Gawani

Genesis 19:15-29, mu ndime yamalembayi tikupezamo zinthu zingapo zokhuza mulungu. Mulungu ndi wolungama ndi wangwiro, sadzalora tchimo lipite osalangidwa. Tikuona mulungu akuchita ntchito yake yopereka chiweruzo pamene akuononga Sodom ndi Gomora. Koma potengera poyamba paja, taona Abrahamu akukambirana ndi mulungu kumupempha kuti asawononge mdzukulu wake Loti. Mulungu akusunga pempho la Abrahamu ndipo akupulumutsa Loti. Izi zikutengera kukhalidwe lina la mulungu, ndipo ndilakuti mulungu ndi wachifundo. Ndipo taona kale akupulumutsa Loti ndi banja lake kuchiweruzo. Kodi kudziwa izi kutanthauzanji kwa Akhristu lero? Tiyenera kukhala opanda chikayiko mwa mulungu. Ngakhale mavuto abwera mulungu adzatipulumutsa ife. Tiyeneranso kupempherera ena mu mpingo ngakhale omwe ali ku mayiko akutali.

Genesis 19:15-29, in this passage we see several things about God. The first thing is, God is just and righteous and he will not let sin go unpunished. We see God exercising his just acts when he destroys Sodom and Gomora. But as seen earlier, Abraham enters a conversation with God asking him to spare his nephew Lot in the judgement. God spares Lot and his family in the judgement. This takes us to another attribute of God which is God is gracious, and we see him keep his promise to spare lot and his family. How does knowing this help Christians today? Well, Christians can rest assured when going through bad conditions and can be confident that God will take care of them just fine. It is the responsibility therefore, of each and every Christian to pray for other Christians in the church and in other parts of the world.