3 | Yesu ndi Mpulumutsi wanu

Gawani

Mulungu adatumiza mwana wake Yesu amene ali Mulungu ndithu komanso Munthu ndithu.

Yesu sadachimwe ingakhalale tchimo lalingóno.

1 Petro 2:22, “Iye sanachite tchimo kapena kunena bodza.”

Yesu adafela machimo athu.

Aroma 5:8, “Koma Mulungu anaonetsa chikondi chake kwa ife chifukwa pamene tinali ochimwabe, Khristu anatifera.”

Mulungu adaukitsa Yesu kwa akufa.

Aroma 6:9, “Pakuti tikudziwa kuti popeza Khristu anaukitsidwa kwa akufa, Iye sangafenso. Imfa ilibenso mphamvu pa Iye.”